ZIONETSERO ZOKAKAMIZA BOMA KUTI LIMANGE MSEWU WA MANGOCHI-MAKANJIRA ZICHTIKA LACHIWIRI LIKUBWERALI.

Gulu lotchedwa Mangochi-Makanjira Road Concerned Citizens lati lachiwiri pa 24 June, lichita zionetsero zofuna kukakamiza boma kuti likwaniritse lonjezano lake lomanga msewu wa Mangochi-Makanjira.

Izi zadza pambuyo pamkumano omwe gululi lachititsa lachisanu pa 20 June, ndi akuluakulu akhonsolo ya Mangochi motsogodzedwa ndi bwanamkubwa a Davie Chigwenembe, a Ernest Kadzokoya omwe ndi mkulu wamzinda wabomali ndinso apolisi.

Poyankhula ndi URS Online ofalitsa nkhani kugululi a Masauko Banda ati mkumanowu wayenda bwino ndipo atsindika kuti zionetserozi zomwe zidzayambire pa round-about ya Bakili Muluzi Highway, kuyambira 9 koloko m’mawa zidzakhala zabata ndi mtendere.

Related posts

MCP TO HOLD A PRESS BRIEFING AIMED TO SHARPENING THE PARTY’S FUTURE.

MKULU WINA WAPHA BAMBO AKE KAAMBA KAMPUNGA.

BOMA LAPEREKA NDALAMA ZOPOSERA K7 MILLION KUTI ZITHANDIZIRE MWAMBO WAMALIRO KWA MZIKA ZOMWE ZINAFA PANGOZI YA BUS.