WACHIWIRI KWAMTSOGOLERI WADZIKO LINO WAFIKA MDZIKO LA MOZAMBIQUE.

Wachiwiri kwamtsogoleri wadziko lino Dr Michael Usi wafika mdziko la Mozambique komwe akakhale nawo pamwambo okumbukira tsiku lomwe dzikolo linalandira Ufulu odzilamulira omwe uchitike lachitatu pa 25 June pa stadium ya Machava mumzinda wa Maputo.

Pofika mdziko la Mozambique a Usi omwe akukaimilira mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus McCathy Chakwera alandilidwa ndi nduna yoona zamaubale amaiko ena a Maria Manuela Dos Santos Lucas komanso kazembe wadziko lino ku Mozambique a Wezi Moyo

Ulendowu boma lati uthandizira kukambirana komanso kulimbitsa ubale wamaiko awiriwa pankhani zamalonda.

Related posts

MCP TO HOLD A PRESS BRIEFING AIMED TO SHARPENING THE PARTY’S FUTURE.

MKULU WINA WAPHA BAMBO AKE KAAMBA KAMPUNGA.

BOMA LAPEREKA NDALAMA ZOPOSERA K7 MILLION KUTI ZITHANDIZIRE MWAMBO WAMALIRO KWA MZIKA ZOMWE ZINAFA PANGOZI YA BUS.