Home Uncategorized MKULU WINA WAPHA BAMBO AKE KAAMBA KAMPUNGA.

MKULU WINA WAPHA BAMBO AKE KAAMBA KAMPUNGA.

by Mclove Mafuta
0 comments

Bambo wina White Mussa wazaka 26 ku Mangochi akuyembekezereka kuyankha mlandu kaamba kopha bambo ake atasemphana maganizo pathumba la mpunga zomwe ndizosemphana ndi gawo 209 loyendetsera malamulo adziko lino.

Ofalitsa nkhani zapolisi m’bomali Inspector Amina Tepan Daud wati izi zachitika usiku wadzulo lachiwiri pa 12 May m’mudzi mwa Maluwa 2 mfumu yaikulu Chowe.

Daud wati malemuwo a George Mussa Mkumba patsikuli anakaniza mwana wawoyo kutenga thumba la mpunga lomwe iye amafuna kutengera mphamvu pomwe amabwelera kwa mkazi wake yemwe anasemphana nae zachitika.Mkangano utakula oganiziridwayu anamenya pamutu bambo akewo ndi chimtengo omwe anakomokeratu pompo ndipo anatera muJira pofika nawo ku chipatala chachikulu cha Mangochi.

White Mussa amachokera m’mudzi mwa Bamusi mfumu yaikulu Chiunda m’boma lomweli la Mangochi.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00