Home Uncategorized BOMA LAPEREKA NDALAMA ZOPOSERA K7 MILLION KUTI ZITHANDIZIRE MWAMBO WAMALIRO KWA MZIKA ZOMWE ZINAFA PANGOZI YA BUS.

BOMA LAPEREKA NDALAMA ZOPOSERA K7 MILLION KUTI ZITHANDIZIRE MWAMBO WAMALIRO KWA MZIKA ZOMWE ZINAFA PANGOZI YA BUS.

by Mclove Mafuta
0 comments

Mtsogoleri wadziko lino Professor Arthur Peter Mutharika wapereka ndalama zokwana K500,000 kwa mawanja 15 omwe achibale awo anafa pangozi ya bus ku Zimbabwe paulendo wawo obwelera kuno kumudzi, kuti ithandizire pamwambo wamaliro.

Wachiwiri kwa mlembi wamkulu kuboma a Stuart Ligomeka anena izi pambuyo pamwambo olandira matupi a anthuwa omwe unachitika usiku wa lolemba pa bwalo la Kamuzu mumzinda wa Blantyre.

M’mawu awo iwo ati a Mutharika ndiokhudzidwa kwambiri ndi imfayi yomwe inachitika kumayambiliro kwa mwezi uno pa 5, ndipo ati ngati dziko lataya mzika zofunika zomwe zikanathandizira dziko lino kutukuka mmagawo osiyanasiyana.

A Ligomeka athokozanso boma la Zimbabwe pantchito yomwe yagwira pothandizira kuti matupiwa afike mdziko muno.

Matupiwa akuyembekezereka kulowa mmanda lero lachiwiri m’madera osiyanasiyana.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00