Home Uncategorized ANA AWIRI AFA ATAGUNDIDWA NDI GALIMOTO KU MANGOCHI.

ANA AWIRI AFA ATAGUNDIDWA NDI GALIMOTO KU MANGOCHI.

by Mclove Mafuta
0 comments

Dalaivala wina alimmanja mwa apolisi ataomba ndikupha ana awiri m’mudzi mwa Sumaili m’boma la Mangochi.

Sharifu Duwa wazaka 10 ndi Kifa Charles wazaka 9 anaombedwa pomwe amaoloka msewu ndi galimoto la mtundu wa Toyota Sienta lomwe limayendetsedwa ndi a Shafi Kassim azaka 28, lolemba pa 11 May 2026, omwe anathawa kusiya galimoto pamalopo zitachitika izi.

Malingana ndi ofalitsa nkhani zapolisi m’bomali Inspector Amina Tepan Daud wati anawo anavulala kwambiri mmutu komanso kuthyoka mafupa amiyendo yakumanzere ndipo anamwalilira munjira pomwe amathamangira nawo ku chipatala cha Namwera Health Centre kuti akalandire thandizo.

A Daud ati m’mawa wa lachiwiri pa 12 May 2026 a Kassim akazipereka okha kupolisi, ndipo akuyembekezereka kuyankha milandu yokupha poyendetsa galimoto mosasamala komanso pokanika kuthandiza anawo powapititsa kuchipatala atagundidwa.

Omwalirawa onse amachokera m’mudzi mwa Salimu mfumu yaikulu Jalasi m’boma lomweli la Mangochi.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00