Home Uncategorized ANTHU OFUNA THANDIZO LA CHITUPA CHOTUKUKIRA MDZIKO ASIMBA LOKOMA.

ANTHU OFUNA THANDIZO LA CHITUPA CHOTUKUKIRA MDZIKO ASIMBA LOKOMA.

by Mclove Mafuta
0 comments

Boma lalamula ofesi ya mnthambi yopanga zitupa zolowera ndi kutulukira mdziko yamumzinda wa Blantyre (Immigration) kuti mwezi uno ukamatha ikhale yatulutsa mlingo wazitupa zosachepera theka la anthu omwe anapereka kale ndalama.

A Norman Chisale omwe ndi wachiwiri kwanduna yoona zachitetezo chamdziko anena izi lero pomwe anayendera ofesi zamnthambiyi.

A Chisale ati mtsogoleri wadziko lino Professor Arthur Peter Mutharika ndi yemwe walamula pofuna kuonetsetsa kuti m’Malawi aliyense yemwe akufuna thandizo la chitupali athandizidwe munthawi yake.

Ndunayi yachenjeza ogwira ntchito kumnthambizi apewe mchitidwe wakatangale maka olandira ndalama zoonjezera panthawi yomwe anthu akufuna thandizoli.

Pakalipano iwo apereka mphamvu kwa anthu ofuna chitupachi kufika kuofesi yawo nthawi iliyonse ngati ogwira ntchito alowetsapo zakatangale Kuti awaneneze.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00