Home Uncategorized A MUTHARIKA APEMPHA MGWIRIZANO PAKATI PAMAIKO AMU SADC KUTI NTCHITO ZACHITUKUKO ZIPITE PATSOGOLO.

A MUTHARIKA APEMPHA MGWIRIZANO PAKATI PAMAIKO AMU SADC KUTI NTCHITO ZACHITUKUKO ZIPITE PATSOGOLO.

by Mclove Mafuta
0 comments

Pulezidenti wadziko lino Professor Arthur Peter Mutharika yemwenso ndi mtsogoleri wamaiko am’chigawo chakum’mwera Kwa Africa (SADC) maka kumnthambi yoona zachitetezo ndi ubale, wapempha maikowa kubwera pamodzi ndi kuchilimika pofuna kupititsa patsogolo ntchito zachitukuko.

A Mutharika anena izi Ku Lilongwe pamkumano wamaikowa omwe unachitikira kunyumba yachifumu ya Kamuzu Palace lachisanu komwe anakumananso ndi atsogoleri akale monga Dr Joyce Banda komanso a Jakaya Kikwete omwe analamulirapo dziko la Tanzania.

Atsogoleri akalewa motsogozedwa ndi a Kikwete, anatsikimizira a Mutharika kuti ntchito yolimbikitsa mtendere wamaiko amu SADC pakali pano ikuyenda bwino maka mmaiko a Democratic Republic of Congo (DRC), Lesotho, Madagascar ndi Mozambique.

Atsogoleriwa ndiomwe akutsogolera komiti ya SADC ya anthu achikulire pomwe a Jakaya Kikwete alikhala pampando pamene Dr Banda ndiomwe ali wachiwiri wawo.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00