MNTHUMWI ZOPOSA 100 ZAPATSIDWA UKADAULO WAMAKONO OYANG’ANIRA CHISANKHO CHAMMAIKO A SADIC

Mlembi wamkulu ku unduna oona zaubale wamaiko akunja (Foreign Affairs) wati ndiokhutira ndimaphunziro anthumwi zamaiko am’chigawo chakum’mwera kwa Africa (SADC) aukadaulo wamakono oyang’anira chisankho chomwe chichitike maiko am’derali.

Dr Mwayiwawo Polepole auza izi Umoyo Radio Online potha pamaphunziro omwe atha lero pa 2 May omwe anayambira pa 28 April pamalo ogona alendo a Capital Hotel mumzinda wa Lilongwe.

M’mawu ake a Terry Rose omwe ndi mkulu oona zandale ku SADC ati mnthumwi zadziko la Malawi zomwe zikhale zikuyang’anira zisankho zamaiko ena monga Zambia,Tanzania ndi Seychelles zapeza ukadaulo okwana obweretsa anthu osiyana pamodzi.

Maphunzirowa mnthumwi zoposa 100 zochokera kuboma,mabungwe oima paokha komanso oimilira zipani ndiomwe anatenga nawo gawo pamaphunziropa

Wolemba : Diffrey Jonathan Bwanaisa – Mangochi

02/05/25

Related posts

https://umoyofm.mw/tigwirizane-polimbana-ndi-hiv/

TIGWIRIZANE POLIMBANA NDI HIV

ANTHU APEMPHEDWA KUSINTHA KAGANIZIDWE PA ZAMATENDA OSAPATSIRANA.

1 comment

Mclove Mafuta May 3, 2025 - 4:24 am
Nice peace
Add Comment