Home Uncategorized KUVOTA KUPITILIRA MPAKA 8 KOLOKO USIKU M’MADERA ENA KU BLANTYRE.

KUVOTA KUPITILIRA MPAKA 8 KOLOKO USIKU M’MADERA ENA KU BLANTYRE.

by Mclove Mafuta
0 comments

Mkulu wa bungwe la Malawi Electoral Commission MEC, a Justice Anabel Mtalimanja akuti kuponya voti Ku Mpata Ku Machinjiri mumzinda wa Blantyre kupitilira mpaka kufika 8 kolok usiku m’malowa.

Izi zili chomwechi kamba ka zovuta zomwe zinachita kum’mawa walero pamene anthu amayamba kuponya voti zinapezeka kuti balot paper imaoneka ngati yochongedwa kale zomwe zinapangitsa chipwilikiti pamalowa.Koma pofufunza ati panali chabe madzi amene anagwelapo.

Ndipo Izi zinapangitsa kuti anthu ayambe kuponya voti mochedwelako patadutsa maola anayi.A wapandowu anenaso kuti anthu 486 omwe maina awo anasowa kaundula boma la thyolo tsopano akwanitsa kuponya voti pamene bungweli linaonjezela nthawi paka 6 koloko.

A Mtalimanja akuyankhula izi pamsonkhano watolankhani omwe uli mkati pakalipano ku BICC mumzinda wa Lilongwe.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00