Home Uncategorized DZIKO LA MALAWI LIKUYEMBEKEZELEKA KUCHITITSA MSONKHANO WAZAMALIMIDWE WA MAIKO AMUNO MU AFRICA

DZIKO LA MALAWI LIKUYEMBEKEZELEKA KUCHITITSA MSONKHANO WAZAMALIMIDWE WA MAIKO AMUNO MU AFRICA

by Mclove Mafuta
0 comments

Unduna wazamalimidwe walengeza kuti uchititsa msonkhano wachisanu ndi chiwiri (7) wasabata yapadera wamaiko amuno mu Africa(Africa-wide Agricultural Extension Week-AAEW) mwezi wamawa.

Nduna ku undunawu a Sam Kawale ati msonkhanowu uchitika kuyambira pa 12 mpaka pa 16 May pa Bingu International Convention Centre (BICC) mumzinda wa Lilongwe.

Msonkhanowu omwe uchitike mogwirizana ndi bungwe la Malawi Forum for Agricultural Advisory Services (AFAAS), at uthandizira kwambiri pobweretsa ukadaulo omwe uchokere kumnthumwi zosiyanasiyana zomwe zifike kumwambowu pansi pamutu oti “kukweza ndi kutukula ntchito zamalonda komanso mafakitale kudzera muzokolora”.

Poyankhula ndi Umoyo Radio Online a Kawale ati mutuwu omwe ulinso mmasomphenya a 2063 otukulira dziko lino uperekanso ukadaulo wina wamakono kudzera mungodya zomwe akambirane.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00