Home Uncategorized BUNGWE LA ESCOM LATHANDIZA AMAYI OPOSA 100 KUMAPHUNZIRO AUKADAULO WALUSO LAMANJA.

BUNGWE LA ESCOM LATHANDIZA AMAYI OPOSA 100 KUMAPHUNZIRO AUKADAULO WALUSO LAMANJA.

by Mclove Mafuta
0 comments

Bungwe lopelekera magetsi la ESCOM Limited, lati ophunzira achizimayi okwana 120 ndiomwe pakalipano la wathandiza kumaphunziro aukadaulo waluso lamanja ngati mbali imodzi yofuna kulimbikitsa kuti pasamakhale kusiyana pakati pa amuna komanso amayi pantchito.

Yemwe akugwilizira ngati mneneri kubungweli a Peter Kanjere anena izi lero pa stadium ya Balaka pamwambo okumbukira tsiku la anthu ogwira ntchito omwe dziko limakhala nalo chaka ndi chaka.

Poyankhula ndi Umoyo Radio Online pambuyo polongosolera mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus McCathy Chakwera zina mwantchito zomwe bungwe lawo limachita, a Kanjere ati bungwe lawo lili ndi ndondomeko zokwanira zoteteza ogwira ntchito awo maka kunkhani yowateteza kunkhanza komanso kuwalimbikitsa amayi kugwira ntchito gawo lililonse powakweza m’maudindo osiyanasiyana.

Dziko la Malawi limakumbulira anthu ogwira ntchito pa 1 May, ndipo mwambo wachaka chino umakumbukilidwa pamutu oti “Ufulu kwaonse ogwira ntchito mozipereka”.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00