Home Uncategorized BANJA LINA ALINJATA LITAPEZEKA NDI MFUTI YOPANDA CHILOLEZO.

BANJA LINA ALINJATA LITAPEZEKA NDI MFUTI YOPANDA CHILOLEZO.

by Mclove Mafuta
0 comments

Banja lina lili m’manja mwa apolisi ku Chiponde m’boma la Mangochi atalipeza ndi mfuti yamtundu wa Pistol yopanda chilolezo.

Malingana ndi mneneri wapolisi m’bomali Inspector Amina Tepan Daudi wati banjali, a Sakina Mustapha ndi a Shukuran Maxon onse azaka 21, awanjata lachinayi pa 17 July pamsika wa Chiponde.

A Daudi ati patsikuli banjali linaba zovala pakaunjika wina pamsikawu, ndipo anthu omwe anaona izi anakwanitsa kugwira mayiyu ndikukampereka ku polisi komwe anapeza mfuti mchikwana chomwe anabisamo zovalazo pofuna kupeza umboni m’menemuu mkuti amuna awo atathawa.

Atafunsidwa zamfutiyo anati ndiyamunawo ndipo mosachedwa apolisi anakagwira bamboyo kunyumba kwake komwe anaulura kuti mfutiyo anaitenga mdziko la South Africa.

Pakalipano banjali likuyembekeza kukaonekera kubwalo la milandu kaamba kopezeka ndi mfuti yopanda chilolezo pambuyo pachipikisheni chomwe apolisi akuchiganizira kuti awiriwa amafuna achitire chiwembu ndi mfutiyo.A Mustapha amachokera m’mudzi mwa Mbalame pomwe a Maxon amachokera m’mudzi mwa Kajeko, mfumu yaikulu Jalasi m’boma lomweli la Mangochi.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00