M’nthambi yoona zachitetezo chandende mdziko muno (Malawi Prison Service) yati posatengera mphekesera zoti asilikali ake ali ndi maganizo onyanyala ntchito, chitetezo chinakali chokhwima m’ndende zonse.
Ofalitsa nkhani ku m’nthambiyi a Steve Meke atsikimizira izi URS potsutsa mphekeserazi kuti ndizabodza ponena kuti asilikaliwa akugwira ntchito yawo popanda chovuta chilichonse.
Ndipo a Meke ati m’nthambiyi ipitiriza kugwira ntchito mwaukadaulo wawo popereka chitetezo kwa a akaidi omwe akusungidwa ndende zamdziko muno.