Home Uncategorized ATOLA NKHANI ALANDILA MAPHUNZIRO

ATOLA NKHANI ALANDILA MAPHUNZIRO

by Mclove Mafuta
0 comments

Bungwe la Center for Social Concerns (CfSC) lawalimbikitsa atolankhani a boma la Mangochi kuti azilemba nkhani zomwe zingabweretse ntendere pakati pa anthu pamene dziko lino likuyembezereka kuchititsa chisankho pa 16 September 2025.

Modzi mwa akulu akulu aku woyang’anira ntchito ku bungweli a Tobias Jere ndi amene wa yakhura izi pa maphunziro a masiku awiri atolankhani a bomali omwe adachitikira pa Holiday Hotel .

A Jere Analangiza atolankhani kuti apewe kulemba nkhani zomwe zingabweletse mpungwe-pungwe ndi mikangano pakati pa a Malawi. komanso kuonetsa mbali polemba nkhani zawo chifukwa zimatha kuwononga tsogolo lawo la utolankhani.

Aisha Silver mmodzi mwa a tolankhani yemwe anali nawo pa maphunzirowa wati maphunzirowa ndi ofunikira kwambiri kwa atolankhani a bomali chifukwa zawalimbikitsa kuti kalembedwe ndi kagwiridwe ntchito kawo kakhale ka ukadawulo popeleka uthenga kwa anthu moyenelera.

Dziko la Malawi likuyembezereka kuchititsa chisankho chosakha mtsogoleri wa dziko, aphungu a ku nyumba ya malamulo komanso ma Khansala pa chisankho chomwe chichitike pa 16 September 2025.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00