Home Uncategorized MAVOTI ADZAWERENGEDWA PAMANJA LATERO BUNGWE LA MEC.

MAVOTI ADZAWERENGEDWA PAMANJA LATERO BUNGWE LA MEC.

by Mclove Mafuta
0 comments

Bungwe loyendetsa chisankho mdziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) lalengeza kuti lidzawerengera mavoti pamanja osati pamakina .

Mai Justice Annabel Mtalimanja omwe ndi wapampando wabungweli, anena izi lero ku Lilongwe, pamwambo otsegulira nyengo yochititsa misonkhano yokopa anthu pachisankho chapa 16 September.

A Mtalimanja ati ntchito yowerengera mavotiyi idzayambira kumalo komwe kwaponyedwa voti kuyambira omwe akupikisana pa mpando wa utsogoleri,aphungu ndi kumalizira makhansala ndipo zonse zidzachitika poyera.

M’mawu awo atatsegulira kampeniyi iwo apempha atsogoleri azipani kuchita misonkhano yawo yokopa anthu mwabata ndi mtendere, posanyadzitsa azipani zina ndipo m’malo make alunjike pamfundo zachitukuko zomwe azikomza zomwe adzachite akapambana.

Bungwe la MEC lati kampeniyi ichitika kwa miyezi iwiri (masiku 60) kuyambira pa 14 July mpaka pa 14 September ndipo lachenjeza kwa onse omwe adzachite misonkhano yawo mosemphana ndi nyengoyi lamulo lidzagwira ntchito.

You may also like

Leave a Comment

Dowa Community Radio is a community-based radio station established in 2020 to be used as a tool of communication in Dowa district and surrounding areas to facilitate issues of Education, gender-based violence, culture, child trafficking, Agriculture, Climate change and environment, transparency and accountability, sports, community self reliance, and many more.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00